Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 19:45-48 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

45. ndi Yehudi, ndi Bene-beraki, ndi Gatirimoni;

46. ndi Me-jarikoni, ndi Rakoni, ndi malire pandunji pajapo.

47. Koma malire a ana a Dani anaturuka kupitirira iwowa; pakuti ana a Dani anakwera nathira nkhondo ku Lesemu, naulanda naukantha ndi lupanga lakuthwa, naulandira, nakhala m'mwemo, naucha Lesemu, Dani; ndilo dzina la Dani atate wao.

48. Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Dani, monga mwa mabanja ao, midzi iyi ndi miraga yao.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 19