Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 18:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Namuka amunawo, napitapita pakati pa dziko, nalilemba m'buku, nayesa midzi yace, magawo asanu, nabwera kwa Yoswa ku cigono ku Silo.

10. Ndipo Yoswa anawalotera maere ku Silo pamaso pa Yehova; ndi apo Yoswa anawagawira ana a Israyeli dziko, monga mwa magawo ao.

11. Ndipo maere a ana a Benjamini anakwera monga mwa mabanja ao; ndi malire a gawo lao anaturuka pakati pa ana a Yuda ndi ana a Yosefe.

12. Ndipo malire ao a kumpoto anacokera ku Yordano; ndi malire anakwera ku mbali ya Yeriko kumpoto, nakwera pakati pa mapiri kumadzulo; ndi maturukiro ace anali ku cipululu ca Beti-aveni.

13. Ndipo malire anapitirirapo kumka ku Luzi, ku mbali ya Luzi, momwemo ndi Beteli, kumwela; ndi malire anatsikira kumka ku Atarotu-adara, ku phiri lokhala kumwela kwa Betihoroni wa kunsi.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 18