Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 17:14-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Pamenepo ana a Yosefe ananena ndi Yoswa, ndi kuti, Watipatsiranji colowa cathu camaere cimodzi ndi gawo limodzi, popeza ife ndife anthu aunyinji, pakuti Yehova anatidalitsa ndi pano pomwe?

15. Ndipo Yoswa ananena nao, Ngati muli anthu aunyinji, kwerani kuli mitengoko, ndi kudziswera minda m'dziko la Aperizi ndi la Arefai; akakuceperani malo ku phiri la Efraimu.

16. Ndipo ana a Yosefe anati, Kuphiriko sikudzatifikira; ndipo Akananionse akukhala m'dziko la cigwa ali nao magareta acitsulo, iwo akukhala m'Bete-Seani, ndi midzi yace ndi iwo omwe akukhala m'cigwa ca Yezereli.

17. Ndipo Yoswa ananena kwa iwo a m'nyumba ya Yosefe, kwa Efraimu ndi Manase, ndi kuti, Inu ndinu anthu aunyinji, muli nayo mphamvu yaikuru; simudzakhala nalo gawo limodzi lokha;

18. koma kuphiriko kudzakhala kwanu pakuti pangakhale mpa mitengo, mudzisweretu minda, ndi maturukiro ace adzakhala anu; pakuti mudzaingitsa Akanani angakhale ali nao magareta acitsulo, angakhale ali amphamvu.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 17