Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 15:11-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. naturuka malire kumka ku mbali ya Ekroni kumpoto; ndipo analemba malire kumka ku Sikeroni, napitirira ku phiri la Baala, naturuka ku Yabindi; ndipo maturukiro a malire anali kunyanja.

12. Ndi malire a kumadzulo anali ku Nyanja Yaikuru ndiwo malire ace. Awa ndi malire a ana a Yuda pozungulira monga mwa mabanja ao.

13. Koma Yoswa anampatsa Kalebe mwana wa Yefune gawo mwa ana a Yuda, monga Yehova adamlamulira, ndiwo mudzi wa Ariba, ndiye atate wa Anaki, ndiwo Hebroni.

14. Ndipo Kalebe anaingitsako ana amuna atatu a Anaki, ndiwo Sesai, ndi Ahimani, ndi Talimai, ana a Anaki.

15. Nakwera komweko kumka kwa nzika za Dibiri; koma kale dzina la Dibiri ndilo Kiriyati-Seferi.

16. Ndipo Kalebe anati, iye amene akantha Kiriyati-Seferi, naulanda, yemweyo ndidzampatsa Akisa mwana wanga akhale mkazi wace.

17. Ndipo Otiniyeli mwana wa Kenazi, mbale wace wa Kalebe, anaulanda; ndipo anampatsa Akisa mwana wace akhale mkazi wace.

18. Ndipo kunali, m'mene anamdzera, anamkangamiza mwamuna wace kuti apemphe atate wace ampatse munda; ndipo anatsika pa buru; pamenepo Kalebe ananena naye, Ufunanji?

19. Nati iye, Mundipatse dalitso; popeza mwandipatsa dziko la kumwela, ndipatseninso zitsime za madzi. Pamenepo anampatsa zitsime za kumtunda, ndi zitsime za kunsi.

20. Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Yuda monga mwa mabanja ao.

21. Ndipo midzi ya ku malekezero a pfuko la ana a Yuda ku malire a Edomu, kumwela ndiwo, Kabizeeli ndi Ederi, ndi Yaguri;

22. ndi Kina ndi Dimona, ndi Adada;

23. ndi Kedesi, ndi Hazori, ndi ltinani;

24. Zifi ndi Telemu ndi Bealoti;

25. ndi Hazorihadata, ndi Kerioti-hezirondi, ndiwo Hazori;

26. Amamu ndi Sema ndi Moloda;

27. ndi Hazara-gada, ndi Hesimoni, ndi Beti-peleti;

28. ndi Hazara-suala, ndi Beereseba, ndi Bizioti;

29. Baala, ndi lyimu, ndi Ezemu;

30. ndi Elitoladi, ndi Kesili ndi Horima;

31. ndi Zikilaga, ndi Madimana ndi Sanasana;

Werengani mutu wathunthu Yoswa 15