13. Pamenepo Yoswa anamdalitsa, napatsa Kalebe mwana wa Yefune Hebroni likhale colowa cace.
14. Cifukwa cace Hebroni likhala colowa cace ca Kalebe mwana wa Yefune Mkenizi mpaka lero lino; popeza anatsata Yehova Mulungu wa Israyeli ndi mtima wonse.
15. Koma kale dzina la Hebroni linali mudzi wa Ariba, ndiye munthu wamkuru pakati pa Aanaki. Ndipo dziko linapumula nkhondo.