Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 14:12-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo tsopano, ndipatseni phiri ili limene Yehova ananenera tsiku lija; pakuti udamva tsiku lijalo kuti Aanaki anali komweko, ndi midzi yaikuru ndi yamalinga; kapena Yehova adzakhala ndi ine, kuti ndiwaingitse monga ananena Yehova.

13. Pamenepo Yoswa anamdalitsa, napatsa Kalebe mwana wa Yefune Hebroni likhale colowa cace.

14. Cifukwa cace Hebroni likhala colowa cace ca Kalebe mwana wa Yefune Mkenizi mpaka lero lino; popeza anatsata Yehova Mulungu wa Israyeli ndi mtima wonse.

15. Koma kale dzina la Hebroni linali mudzi wa Ariba, ndiye munthu wamkuru pakati pa Aanaki. Ndipo dziko linapumula nkhondo.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 14