23. Ndipo malire a ana a Rubeni ndiwo Yordano ndi malire ace. Ndico colandira ca ana a Rubeni monga mwa mabanja ao, midzi yace ndi miraga yace.
24. Ndipo Mose anapatsira pfuko la Gadi, ana a Gadi, monga mwa mabanja ao.
25. Ndipo malire ao ndiwo Yazeri, ndi midzi yonse ya Gileadi, ndi dziko la ana a Amoni logawika pakati, mpaka ku Aroeri, wokhala cakuno ca Raba;
26. ndi kuyambira Hesiboni mpaka Ramati-Mizipe, ndi Betonimu; ndi kuyambira Mahanaimu mpaka malire a Dibiri;