Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 12:6-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Mose mtumiki wa Yehova ndi ana a Israyeli anawakantha; ndi Mose mtumiki wa Yehova analipereka kwa Arubeni, ndi Agadi ndi pfuko la Manase logawika pakati, likhale colowacao.

7. Ndipo awa ndi mafumu a dzikolo amene Yoswa ndi ana a Israyeli anawakantha tsidya lija la Yordano kumadzulo, kuyambira Baala-gadi m'cigwa ca Lebano mpaka phiri la Halaki lokwera kumka ku Seiri; ndipo Yoswa analipereka kwa mapfuko a Israyeli, likhale lao lao, monga mwa magawo ao;

8. kumapiri ndi kucigwa, ndi kucidikha, ndi kumatsikiro, ndi kucipululu, ndi kumwela: Ahiti, Aamori, ndi Akanani, Aperizi, Ahivi ndi Ayebusi:

9. mfumu ya ku Yeriko, imodzi; mfumu ya ku Ai, ndiwo m'mbali mwa Beteli, imodzi;

10. mfumu ya ku Yerusalemu, imodzi; mfumu ya ku Hebroni, imodzi; mfumu ya ku Yarimutu, imodzi;

11. mfumu ya ku Lakisi, imodzi;

12. mfumu ya ku Egiloni, imodzi; mfumu ya ku Gezere, imodzi;

13. mfumu ya ku Dibiri, imodzi; mfumu ya ku Gederi, imodzi;

14. mfumu ya ku Horima, imodzi; mfumu ya ku Haradi, imodzi;

15. mfumu ya ku Libina, imodzi; mfumu ya ku Adulamu, imodzi;

16. mfumu ya ku Makeda, imodzi; mfumu ya ku Beteli, imodzi;

17. mfumu ya ku Tapuwa, imodzi; mfumu ya ku Heferi, imodzi;

18. mfumu ya ku Afeki, imodzi; mfumu ya ku Lasaroni, imodzi;

19. mfumu ya ku Madoni, imodzi; mfumu ya ku Hazori, imodzi;

Werengani mutu wathunthu Yoswa 12