Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 11:21-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo Yoswa anadza nthawi yomweyo, napasula Aanaki kuwacotsa kumapiri, ku Hebroni, ku Dibiri, ku Anabi, ndi ku mapiri onse a Yuda, ndi ku mapiri onse a Israyeli; Yoswa anawaononga konse, ndi midzi yao yomwe.

22. Panalibe Aanaki otsala m'dziko la ana a Israyeli; koma m'Gaza, ndi m'Gati ndi m'Asidodo anatsalamo ena.

23. Motero Yoswa analanda dziko lonse monga mwa zonse Yehova adazinena kwa Mose; ndipo Yoswa analipereka kwa Israyeli, likhale lao lao, pfuko liri lonse gawo lace. Ndipo dziko linapumula nkhondo.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 11