Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 11:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali, pamene Yabini mfumu ya ku Hazoro anacimva, anatwna kwa Yabobu mfumu ya ku Madoni, ndi kwa mfumu ya ku Simironi, ndi kwa mfumu ya ku Akasafu,

2. ndi kwa mafwnu akukhala kumpoto kumapiri, ndi kucigwa kwumwela kwa Kineroto, ndi kucidikha, ndi ku mitunda ya Doro kwnadzulo;

3. kwa Akanani kwn'mawa ndi kumadzulo, ndi kwa Aamori ndi Ahiti, ndi Aperizi ndi Ayebusi kumapiri, ndi kwa Ahivi kunsi kwa Herimoni, m'dziko la Mizipa.

4. Ndipo anaturuka, iwo ndi makamu ao onse nao, anthu ambiri, kucuruka kwao ngati mcenga uli m'mphepete mwa nyanja; ndi akavalo ndi magareta ambirimbiri.

5. Ndipo mafwnu awa onse anasonkhana, nadza namanga pamodzi ku madzi a Meromu, kumthira Israyeli nkhondo.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 11