Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 10:35-39 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

35. Naulanda tsiku lomwelo, naukantha ndi lupanga lakuthwa, nawaononga konse amoyo onse anali m'mwemo tsiku lomwelo, monga mwa zonse anacitira Lakisi.

36. Ndipo Yoswa ndi Aisrayeli onse naye anakwera kucokera ku Egiloni mpaka ku Hebroni, nauthira nkhondo;

37. naulanda, naukantha ndi lupanga lakuthwa, ndi mfumu yace ndi midzi yace yonse, ndi amoyo onse anali m'mwemo, osasiyapo ndi mmodzi yense, monga mwa zonse anacitira Egiloni; koma anauononga konse, ndi amoyo onse anali m'mwemo.

38. Pamenepo Yoswa, ndi Aisrayeli onse naye, anabwerera kudza ku Dibiri, nauthira nkhondo,

39. naulanda, ndi mfumu yace ndi midzi yace yonse; naikantha ndi lupanga lakuthwa, naononga konse amoyo onse anali m'mwemo; sanasiya ndi mmodzi yense; monga anacitira Hebroni momwemo anacitira Dibiri ndi mfumu yace, monganso anacitira Libina ndi mfumu yace.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 10