Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 10:22-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Pamenepo Yoswa anati, Tsegula pakamwa pa phanga ndi kunditurutsira m'phanga mafumu asanuwo.

23. Ndipo anatero, naturutsira m'phanga mafumu asanuwo, mfumu ya ku Yerusalemu, mfumu ya ku Hebroni, mfumu ya ku Yarimutu, mfumu ya ku Lakisi, mfumu ya ku Egiloni.

24. Ndipo kunali, ataturutsira Yoswa mafumu awa, Yoswa anaitana amuna onse a Israyeli, ndipo anati kwa akazembe a anthu a nkhondo amene anamuka naye, Yandikirani, pondani pa makosi a mafumu awa. Nayandikira iwo, naponda pa makosi ao.

25. Pamenepo Yoswa ananena nao, Musaope, musatenge nkhawa; khalani amphamvu, nimulimbike mtima; pakuti Yehova adzatero ndi adani: anu onse amene mugwirana nao: nkhondo.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 10