Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 14:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Munthu wobadwa ndi mkaziNgwa masiku owerengeka, nakhuta mabvuto,

2. Aturuka ngati duwa, nafota;Athawa ngati mthunzi, osakhalitsa.

3. Ndipo kodi mumtsegulira maso anu wotereyo,Ndi kunditenga kunena nane mlandu Inu?

4. Adzaturutsa coyera m'cinthu codetsa ndani? nnena mmodzi yense.

5. Popeza masiku ace alembedwa, ciwerengo ca miyezi yace cikhala ndi Inu,Ndipo mwamlembera malire ace, kuti asapitirirepo iye;

6. Mumleke osamthira maso, kuti apumule,Kuti akondwere nalo tsiku lace monga wolembedwa nchito.

7. Pakuti akaulikha mtengo pali ciyembekezo kuti udzaphukanso,Ndi kuti nthambi yace yanthete siidzasowa.

8. Ngakhale muzu wace wakalamba m'nthaka,Ndi tsinde lace likufa pansi;

Werengani mutu wathunthu Yobu 14