Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 8:7-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. cifukwa cace, taonani, Ambuye atengera pa iwo madzi a Nyanja, olimba ndi ambiri, kunena mfumu ya Asuri ndi ulemerero wace wonse; ndipo iye adzadzala mphaluka zace zonse, nadzasefukira pamtunda ponse.

8. Ndipo iye adzapitapitakulowa m'Yuda; adzasefukira, napitirira; adzafikira m'khosi; ndi kutambasula kwa mapiko ace, kudzakwanira dziko lanu m'citando mwace, inu Imanueli.

9. Citani phokoso, anthu inu, koma mudzatyokatyoka; cherani khutu, inu nonse a maiko akutari; kwindani nokha, koma mudzatyokatyoka; kwindani nokha, koma mudzatyokatyoka.

10. Panganani upo, koma udzakhala cabe; nenani mau, koma sadzacitika; pakuti Mulungu ali pamodzi ndi ife.

11. Pakuti Yehova watero kwa ine ndi dzanja lolimba, nandilangiza ine kuti ndisayende m'njira ya anthu awa, nati,

12. Musacinene, Ciwembu; ciri conse cimene anthu awa adzacinena, Ciwembu; musaope monga kuopa kwao kapena musacite mantha.

13. Yehova wa makamu, Iye mudzamyeretsa; muope Iye, akucititseni mantha Iye.

14. Ndipo Iye adzakhala malo opatulika; koma mwala wopunthwitsa, ndi thanthwe lolakwitsa la nyumba zonse ziwiri za Israyeli, khwekhwe ndi msampha wa okhala m'Yerusalemu.

15. Ndipo ambiri adzapunthwapo, nagwa, natyoka, nakodwa, natengedwa.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 8