Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 63:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Pakuti tsiku lakubwezera liri mumtima mwanga, ndi caka ca kuombola anthu anga cafika.

5. Ndipo ndinayang'ana, koma panalibe wothangata; ndipo ndinadabwa kuti panalibe wocirikiza; cifukwa cace mkono wanga wanga unanditengera cipulumutso, ndi ukali wanga unandicirikiza Ine.

6. Ndipo ndinapondereza anthu m'kukwiya kwanga, ndi kuwatswanya mu ukali wanga, ndi kutsanulira mwazi wa moyo wao.

7. Ndidzachula za cifundo cace ca Yehova, ndi matamando a Yehova, monga mwa zonse zimene Yehova wapereka kwa ife; ndi ubwino wace waukuru kwa banja la Israyeli, umene Iye wapereka kwa iwo, monga mwa cifundo cace, ndi monga mwa nchito zocuruka za cikondi cace.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 63