Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 62:6-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndaika alonda pa malinga ako, Yerusalemu; iwo sadzakhala cete usana pena usiku; inu akukumbutsa Yehova musakhale cete,

7. ndipo musamlole akhale cete, kufikira Iye atakhazikitsa naika Yerusalemu akhale tamando m'dziko lapansi.

8. Yehova analumbira pa dzanja lace lamanja, ndi mkono wace wamphamvu, Zoonadi, sindidzaperekanso tirigu wako akhale cakudya ca adani ako, ndipo alendo sadzamwa vinyo wako amene iwe unagwirira nchito;

9. koma iwo amene adzakolola adzadya ndi kutamanda Yehova; ndi iwo amene adzamchera adzamumwa m'mabwalo a kacisi wanga.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 62