15. Inde coona cisoweka; iye amene asiya coipa, zifunkhidwa zace; ndipo Yehova anaona ici, ndipo cidamuipira kuti palibe ciweruzo.
16. Ndipo Iye anaona kuti palibe munthu, nazizwa kuti palibe wopembedzera; cifukwa cace mkono wace wace unadzitengera yekha cipulumutso; ndi cilungamo cace cinamcirikiza.
17. Ndipo anabvala cilungamo monga cida ca pacifuwa, ndi cisoti ca cipulumutso pamutu pace; nabvala zobvala zakubwezera cilango, nabvekedwa ndi cangu monga copfunda,
18. Monga mwa nchito zao momwemo Iye adzabwezera amaliwongo ace ukali, nadzabwezera adani ace cilango; nadzabwezeranso zisumbu cilango.
19. Comweco iwo adzaopa dzina la Yehova kucokera kumadzulo, ndi ulemerero wace kumene kuturukira dzuwa; pakuti pamene mdani adzafika ngati cigumula, mzimu wa Yehova udzamkwezera mbendera yomletsa.
20. Ndipo Mombolo adzafika ku Ziyoni, ndi kwa iwo amene atembenuka kusiya kulakwa mwa Yakobo, ati Yehova.