Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 58:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Kodi si ndiko kupatsa cakudya cako kwa anjala, ndi kuti ubwere nao kunyumba kwako aumphawi otayika? pakuona wamalisece kuti umbveke, ndi kuti usadzibisire wekha a cibale cako?

8. Pomwepo kuunika kwako kudzawalitsa monga m'mawa, ndi kucira kwako kudzaonekera msanga msanga; ndipo cilungamo cako cidzakutsogolera; ulemerero wa Yehova udzakhala wocinjiriza pambuyo pako.

9. Pamenepo udzaitana, ndipo Yehova adzayankha; udzapfuula ndipo Iye adzati, Ndine pano. Ngati ucotsa pakati pa iwe gori, kukodolana moipa, ndi kulankhula moipa,

10. ndipo ngati upereka kwa wanjala cimene moyo Iwako umakhumba, ndi kukhutitsa moyo wobvutidwa, pomwepo kuunika kwako kudzauka mumdima, ndipo usiku wako udzanga usana;

Werengani mutu wathunthu Yesaya 58