12. Ndipo iwo amene adzakhala a iwe adzamanga malo akale abwinja; udzautsa maziko a mibadwo yambiri; udzachedwa Wokonza pogumuka, Wakubwezera njira zakukhalamo.
13. Ukaletsa phazi lako pa Sabata, ndi kusiya kucita kukondwerera kwako tsiku: langa lopatulika, ndi kuyesa Sabata tsiku lokondwa lopatulika la Yehova, lolemekezeka, ndipo ukalilemekeza ilo, osacita njira zako zokha, osafuna kukondwa kwako kokha, osalankhula mau ako okha;
14. pomwepo udzakondwa mwa Yehova; ndipo Ine ndidzakuyendetsa pa misanje ya dziko lapansi; ndipo ndidzakudyetsa colowa ca kholo lako Yakobo; pakuti pakamwa pa Yehova pananenapo.