Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 57:5-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Inu amene muutsa zilakolako zanu pakati pa mathundu, patsinde pa mitengo yonse ya gudugudu, amene mupha ana m'zigwa pansi pa mapanga a matanthwe?

6. Pakuti pa miyala yosalala ya m'cigwa pali gawo lako; iyo ndiyo gawo lako; ndiyo imene unaitsanulirira nsembe yothira, ndi kupereka nsembe yaufa. Kodi ndidzapembedzedwa pa zinthu zimenezi?

7. Pamwamba pa phiri lalitaritari unayala mphasa yako; kumenekonso wakwera kukapereka nsembe.

8. Ndi kumbuyo kwa zitseko ndi mphuthu waimiritsa cikumbutso cako, pakuti wadzionetsa wekha kwa wina, wosati kwa Ine; ndipo wakwerako, wakuza mphasa yako, ndi kupangana nao pangano; unakonda mphasa yao kumene unaiona.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 57