Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 57:16-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Pakuti sindidzatsutsana ku nthawi zonse, sindidzakwiya masiku onse; pakuti mzimu udzalefuka pamaso pa Ine, ndi miyoyo imene ndinailenga.

17. Cifukwa ca kuipa kwa kusirira kwace ndinakwiya ndi kummenya iye; ndinabisa nkhope yanga, ndipo ndinakwiya; ndipo iye anankabe mokhota m'njira ya mtima wace.

18. Ndaona njira zace, ndipo ndidzamciritsa; ndidzamtsogoleranso, ndi kumbwezera iye ndi olira maliro ace zotonthoza mtima.

19. Ndilenga cipatso ca milomo, Mtendere, mtendere kwa iye amene ali kutari, ndi kwa iye amene ali cifupi, ati Yehova; ndipo ndidzamciritsa iye.

20. Koma oipa ali ofanana ndi nyanja yowinduka; pakuti siingapume, ndi madzi ace autsa matope ndi ubve.

21. Palibe mtendere, ati Mulungu wanga, kwa oipa.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 57