16. Pakuti sindidzatsutsana ku nthawi zonse, sindidzakwiya masiku onse; pakuti mzimu udzalefuka pamaso pa Ine, ndi miyoyo imene ndinailenga.
17. Cifukwa ca kuipa kwa kusirira kwace ndinakwiya ndi kummenya iye; ndinabisa nkhope yanga, ndipo ndinakwiya; ndipo iye anankabe mokhota m'njira ya mtima wace.
18. Ndaona njira zace, ndipo ndidzamciritsa; ndidzamtsogoleranso, ndi kumbwezera iye ndi olira maliro ace zotonthoza mtima.
19. Ndilenga cipatso ca milomo, Mtendere, mtendere kwa iye amene ali kutari, ndi kwa iye amene ali cifupi, ati Yehova; ndipo ndidzamciritsa iye.
20. Koma oipa ali ofanana ndi nyanja yowinduka; pakuti siingapume, ndi madzi ace autsa matope ndi ubve.
21. Palibe mtendere, ati Mulungu wanga, kwa oipa.