Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 56:4-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Pakuti atero Yehova kwa mifule imene isunga masabata, nisankha zinthu zimene zindikondweretsa Ine, nigwira zolimba cipangano canga,

5. Kwa iyo ndidzapatsa m'nyumba yanga ndi m'kati mwa makoma anga malo, ndi dzina loposa la ana amuna ndi akazi; ndidzawapatsa dzina lacikhalire limene silidzadulidwa.

6. Alendonso amene adziphatika okha kwa Yehova, kuti amtumikire Iye, ndi kukonda dzina la Yehova, akhale atumiki ace, yense amene asunga sabata osaliipitsa, nagwira zolimba cipangano canga;

7. naonso ndidzanka nao ku phiri langa lopatulika, ndi kuwasangalatsa m'nyumba yanga yopemphereramo; zopereka zao zopsereza ndi nsembe zao zidzalandiridwa pa guwa la nsembe langa; pakuti nyumba yanga idzachedwa nyumba yopemphereramo anthu onse.

8. Ambuye Yehova amene asonkhanitsa otayika a Israyeli ati, Komabe ndidzasonkhanitsa ena kwa iye, pamodzi ndi osonkhanitsidwa ace ace.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 56