Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 54:10-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Pakuti mapiri adzacoka, ndi zitunda zidzasunthika; koma kukoma mtima kwanga sikudzakucokera iwe, kapena kusunthika cipangano canga ca mtendere, ati Yehova amene wakucitira iwe cifundo.

11. Iwe wosautsidwa, wobelukabeluka ndi namondwe, wosatonthola mtima, taona, ndidzakhazika miyala yako m'maanga-maanga abwino, ndi kukhazika maziko ako ndi masafiro.

12. Ndipo ndidzamanga mazenera ako ndi miyala yofiira, ndi zipata zako ndi bareketi, ndi malire ako onse ndi miyala yokondweretsa.

13. Ndipo ana ako onse adzaphunzitsidwa ndi Yehova; ndipo mtendere wa ana ako udzakhala waukulu.

14. M'cilungamo iwe udzakhazikitsidwa, udzakhala kutari ndi cipsinjo, pakuti sudzaopa; udzakhala kutari ndi mantha, pakuti sadzafika cifupi ndi iwe.

15. Taona, iwo angasonkhanitse pamodzi, koma si ndi Ine; amene ali yense adzasonkhana pamodzi akangane ndi iwe adzagwa cifukwa ca iwe.

16. Taona, ndalenga wacipala amene abvukuta moto wamakala, ndi kuturutsamo cida ca nchito yace; ndipo ndalenga woononga kuti apasule.

17. Palibe cida cosulidwira iwe cidzapindula; ndipo lilime lonse limene lidzakangana nawe m'ciweruzo udzalitsutsa. Ici ndi colowa ca atumiki a Yehova, ndi cilungamo cao cimene cifuma kwa Ine, ati Yehova.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 54