Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 53:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndani wamvera uthenga wathu? Ndi mkono wa Yehova wabvumbulukira yani?

2. Pakuti ameneyo adzaphuka pamaso pace ngati mtengo wanthete, ndi ngati muzu womera m'nthaka youma; Iye alibe maonekedwe, pena kukongola; ndipo pamene timuona palibe kukongola kuti timkhumbe.

3. Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu; munthu wazisoni, ndi wodziwa zowawa; ndipo ananyozedwa monga munthu wombisira anthu nkhope zao; ndipo ife sitinamlemekeza.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 53