Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 5:1-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndiyimbire wokondedwa wanga nyimbo ya wokondedwa wanga ya munda wace wamphesa, Wokondedwa wanga anali ndi munda wamphesa m'citunda ca zipatso zambiri;

2. ndipo iye anakumba mcerenje kuzungulira kwete, natolatola miyala pamenepo naokapo mpesa wosankhika, namangapo pakati pace nsanja, nasema mopondera mphesa, nayembekeza kuti udzabala mphesa, koma unangobala mphesa zosadya.

3. Ndipo tsopano, inu okhala m'Yerusalemu, ndi anthu a Yuda, weruzanitu mlandu wa ine ndi munda wanga wamphesa.

4. Ndikanacitanso ciani ndi munda wanga wamphesa, cimene sindinacite m'menemo; muja ndinayembekeza kuti udzabala mphesa, wabaliranji mphesa zosadya?

5. Ndipo tsopano ndidzakuuzani cimene nditi ndicite ndi munda wanga wamphesa; ndidzacotsapo chinga lace, ndipo zidzadyedwa; ndidzagumula linga lace, ndipo zidzapondedwa pansi;

6. ndipo ndidzaupasula; sudzadzomboleredwa kapena kulimidwa; koma padzamera lunguzi ndi minga; ndidzalamuliranso mitambo kuti isabvumbwepo mvula.

7. Cifukwa kuti munda wamphesa wa Yehova wa makamu ndiwo banja la Israyeli, ndi anthu a Yuda, mtengo wace womkondweretsa; Iye anayembekeza ciweruziro, koma onani kuphana; nayembekeza cilungamo, koma onani kupfuula.

8. Tsoka kwa iwo amene aphatikiza nyumba ndi nyumba, amene alumikiza munda ndi munda, kufikira padzapanda malo, ndipo inu mudzasiyidwa nokha pakati pa dziko!

9. M'makutu anga, ati Yehova wa makamu, Zoonadi nyumba zambiri zidzakhala bwinja, ngakhale zazikuru ndi zokoma zopanda wokhalamo.

10. Cifukwa kuti munda wamphesa wa madera khumi udzangobala mbiya imodzi, ndi mbeu za nsengwa khumi zidzangobala nsengwa imodzi.

11. Tsoka kwa iwo amene adzuka m'mamawa kuti atsate zakumwa zaukali; amene acezera usiku kufikira vinyo awaledzeretsal

12. Ndipo zeze ndi mgoli, ndi lingaka ndi citoliro, ndi vinyo, ziri m'mapwando ao; koma iwo sapenyetsa nchito ya Yehova; ngakhale kuyang'ana pa macitidwe a manja ace.

13. Cifukwa cace anthu anga amuka m'nsinga, cifukwa ca kusowa nzeru; ndi amuna ao olemekezeka ali ndi njala, ndi khamu lao lauma kukhosi.

14. Ndipo manda akuza cilakolako cace, natsegula kukamwa kwace kosayeseka; ndi ulemerero wao, ndi unyinji wao, ndi phokoso lao, ndi iye amene akondwerera mwa iwo atsikira mommo.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 5