Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 49:15-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Kodi mkazi angaiwale mwana wace wa pabere, kuti iye sangacitire cifundo mwana wombala iye? inde awa angaiwale, koma Ine sindingaiwale iwe.

16. Taona ndakulembera iwe pa zikhato za manja anga; makoma ako alipo masiku onse pamaso panga,

17. Ana ako afulumira; opasula ako ndi iwo amene anakusakaza adzacoka pa iwe.

18. Tukula maso ako kuunguza-unguza, nuone; onsewa asonkhana pamodzi, nadza kwa iwe. Pali Ine, ati Yehova, iwe ndithu udzadzibveka wekha ndi iwo onse, monga ndi cokometsera, ndi kudzimangira nao m'cuuno ngati mkwatibwi.

19. Pakuti, kunena za tnalo ako osiyidwa ndi abwinja ndi dziko lako limene lapasulidwa tsopano, ndithu iwe udzakhala wocepera okhalamo, ndi iwo amene anakumeza iwe adzakhala kutari.

20. Ana ako amasiye adzanena m'makutu ako, Malo andicepera ine, ndipatse malo, kuti ndikhalemo.

21. Pamenepo udzati m'mtima mwako, Ndani wandibalitsa ine amenewa, popeza ana anga anacotsedwa kwa ine, ndipo ndiri wouma, ndi wocotsedwa m'dziko, ndi woyendayenda kwina ndi kwina? ndipo ndani wadza ndi awa? Taona ndinasiyidwa ndekha, amenewa anali kuti?

Werengani mutu wathunthu Yesaya 49