Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 43:9-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Amitundu onse asonkhane pamodzi, ndi anthu aunjikane; ndani mwa iwo anganene ici ndi kuonetsa ife zinthu zakale? atenge mboni zao, kuti abvomerezeke ndi olungama; pena amve, nanene zoonadi.

10. Inu ndinu mboni zanga, ati Yehova, ndi mtumiki wanga, amene ndakusankha; kuti mundidziwe, ndi kundikhulupirira Ine, ndi kuzindikira, kuti Ine ndine; ndisanakhale Ine, panalibe Mulungu wolengedwa, ngakhale pambuyo panga sipadzakhala wina.

11. Ine, Inetu ndine Yehova; ndipo palibe Mpulumutsi, koma Ine ndekha.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 43