Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 43:6-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ine ndidzati ndi kumpoto, Pereka; ndi kumwera, Usaletse; bwera nao ana anga amuna kucokera kutari, ndi ana anga akazi kucokera ku malekezero a dziko lapansi;

7. yense wochedwa dzina langa, amene ndinamlenga cifukwa ca ulemerero wanga; ndinamuumba iye; inde, ndinampanga iye.

8. Turutsani anthu akhungu, amene ali ndi maso, ndi agonthi, amene ali ndi makutu.

9. Amitundu onse asonkhane pamodzi, ndi anthu aunjikane; ndani mwa iwo anganene ici ndi kuonetsa ife zinthu zakale? atenge mboni zao, kuti abvomerezeke ndi olungama; pena amve, nanene zoonadi.

10. Inu ndinu mboni zanga, ati Yehova, ndi mtumiki wanga, amene ndakusankha; kuti mundidziwe, ndi kundikhulupirira Ine, ndi kuzindikira, kuti Ine ndine; ndisanakhale Ine, panalibe Mulungu wolengedwa, ngakhale pambuyo panga sipadzakhala wina.

11. Ine, Inetu ndine Yehova; ndipo palibe Mpulumutsi, koma Ine ndekha.

12. Ine ndalalikira, ndipo ndikupulumutsa ndi kumvetsa, ndipo panalibe Mulungu wacilendo pakati pa inu; cifukwa cace inu ndinu mboni zanga, ati Yehova, ndipo Ine ndine Mulungu.

13. Inde ciyambire nthawi Ine ndine, ndipo palibe wina wopulumutsa m'dzanja langa; ndidzagwira nchito, ndipo ndani adzaletsa?

14. Atero Yehova, Mombolo wanu, Woyera wa Israyeli: Cifukwa ca inu ndatumiza ku Babulo, ndipo ndidzatsitsira iwo onse monga othawa, ngakhale Akasidi m'ngalawa za kukondwa kwao.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 43