Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 42:16-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndipo ndidzayendetsa akhungu m'khwalala, limene iwo salidziwa; m'njira zimene iwo sazidziwa ndidzawatsogolera; ndidzawalitsa mdima m'tsogolo mwao, ndi kulungamitsa malo okhota. Zinthu Izi ine ndidzacita, ndipo sindidzawasiya.

17. Iwo adzabwezedwa m'mbuyo, adzakhala ndi manyazi ambiri amene akhulupirira mafano osemedwa, nati kwa mafano oyengeka, Inu ndinu milungu yathu.

18. Imvani, agonthi inu; yang'anani, akhungu inu, kuti muone.

19. Ndani ali wakhungu, koma mtumiki wanga? pena wagonthi, monga mthenga wanga, amene ndimtumiza? ndani ali wakhungu monga bwenzi langa, ndi wakhungu monga mtumiki wa Yehova?

20. Iwe waona zinthu zambiri, koma susamalira konse; makutu ako ali otseguka, koma sumva konse.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 42