Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 36:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma panali caka cakhumi ndi cinai ca mfumu Hezekiya, Sanakeribu, mfumu ya Asuri anadza, nathira nkhondo pa midzi ya malinga yonse ya Yuda, nailanda.

2. Ndipo mfumu ya Asuri inatumiza kazembe kucokera pa Lakisi, kunka ku Yerusalemu, kwa mfumu Hezekiya, ndi nkhondo yambiri. Ndipo iye anaima cifupi ndi mcerenje wa thamanda la kumtunda, m'khwalala la pa mwaniko wa wotsuka nsaru.

3. Ndipo anamturukira Eliakimu, mwana wa Hilikiya, amene anali wapanyumba, ndi Sebina, mlembi, ndi Yoaki, mwana wa Asafu, mkumbutsi.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 36