Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 34:6-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Lupanga la Yehova lakhuta ndi mwazi, lanona ndi mafuta ndi mwazi wa ana a nkhosa, ndi mbuzi, ndi mafuta a imso ya nkhosa zamphongo; pakuti Yehova ali ndi nsembe m'Bozira, ndi ophedwa ambiri m'dziko la Edomu.

7. Ndipo njati zidzatsika ndi iwo, ndi ng'ombe zofula ndi zamphongo; ndi dziko lao lidzakhuta ndi mwazi, ndi pfumbi lao lidzanona ndi mafuta.

8. Pakuti liri tsiku la kubwezera la Yehova, caka cakubwezera cilango, mlandu wa Ziyoni.

9. Ndipo mitsinjeyo idzasanduka matope akuda, ndi pfumbilo lidzasanduka suifure, ndi dziko lacelo lidzasanduka matope oyaka moto.

10. Sadzazimikai usiku, ngakhale usana; utsi wace udzakwera nthawi zonse; m'mibadwo mibadwo lidzakhala labwinja, palibe amene adzapitapo nthawi za nthawi.

11. Koma bvuo ndi nungu zidzakhalamo, ndipo kadzidzi ndi khungubwi adzakhala m'menemo, ndipo Mulungu adzatambalika pamenepo cingwe coongolera ca cisokonezo, ndi cingwe colungamitsa ciriri cosatha kucita kanthu.

12. Iwo adzaitana mfulu zace zilowe m'ufumu, koma sizidzaonekako; ndi akalonga ace onse adzakhala cabe.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 34