Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 30:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Tsoka okhulupirira Aigupto. Tsoka kwa ana opanduka, ati Yehova, amene atenga uphungu koma si pa Ine; napangana pangano opanda mzimu wanga, kuti aonjezere cimo ndi cimo;

2. amene ayenda kutsikira ku Aigupto, osafunsa kukamwa kwanga, kudzilimbitsa iwo okha ndi li mphamvu za Farao, ndi kukhulupirira mthunzi wa Aigupto

3. Cifukwa cace mphamvu za Farao zidzakhala kwa inu manyazi, ndi kukhulupirira mthunzi wa Aigupto kudzakhala cisokonezo canu.

4. Pakuti akalonga ace ali pa Zaani, ndi mithenga yace yafika ku Hanesi.

5. Iwo onse adzakhala ndi manyazi, ndi anthu amene sangapindule nao kanthu, amene sakhala kwa iwo thangata, pena phindu, koma manyazi ndi citonzo.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 30