Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 29:18-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo tsiku limenelo gonthi adzam va mau a m'buku, ndi maso akhungu adzaona poturuka m'zoziya ndi mumdima.

19. Ofatsanso kukondwa kwao kudzacuruka mwa Yehova, ndi aumphawi a mwa anthu adzakondwerera mwa Woyera wa Israyeli.

20. Pakuti woopsya wagoma, ndi wonyoza watha, ndi onse odikira zolakwa alikhidwa;

21. amene apalamulitsa munthu mlandu, namchera msampha iye amene adzudzula pacipata, nambweza wolungama ndi cinthu cacabe.

22. Cifukwa cace Yehova amene anaombola Abrahamu, atero za banja la Yakobo: Yakobo sadzakhala ndi manyazi tsopano, ngakhale nkhope yace tsopano sidzagwa.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 29