Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 26:15-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Mwacurukitsa mtundu, Yehova, mwacurukitsa mtundu; Inu mwalemekezeka, mwakuza malire onse a dziko.

16. Yehova, iwo adza kwa Inu mobvutika, iwo anathira pemphero, muja munalikuwalanga.

17. Monga ngati mkazi wokhala ndi pakati, amene nthawi yace yakubala yayandikira, amva zopweteka, ndi kupfuula m'zowawa zace; momwemo takhala ife pamaso panu, Yehova.

18. Ife tinali ndi pakati, ife tinamva zopweteka, tafanana ngati tabala mphepo; sitinacite cipulumutso ciri conse pa dziko lapansi; ngakhale okhala m'dziko lapansi sanagwe.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 26