Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 24:5-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Dzikonso laipitsidwa ndi okhalamo ace omwe, cifukwa iwo alakwa pamalamulo nasinthanitsa malemba, natyola cipangano ca nthawi zonse.

6. Cifukwa cace citemberero cadya dziko, ndi amene akhala m'menemo apezedwa ocimwa, cifukwa cace okhalamo a padziko atenthedwa, ndipo anthu owerengeka atsala.

7. Vinyo watsopano alira, mpesa ulefuka, mitima yonse yokondwa iusa moyo.

8. Kusangalala kwa mangaka kwalekeka, phokoso la iwo amene aserera litha, kukondwa kwa mngoli kwalekeka.

9. Iwo sadzamwa vinyo ndi kuyimba nyimbo; cakumwa caukali cidzawawa kwa iwo amene acimwa.

10. Mudzi wosokonezeka wagwetsedwa pansi; nyumba zonse zatsekedwa, kuti asalowemo munthu.

11. Muli mpfuu m'makwalala cifukwa ca vinyo; kukondwa konse kwadetsedwa, kusangalala kwa dziko kwatha.

12. M'mudzi mwatsala bwinja, ndi cipata camenyedwa ndi cipasuko.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 24