Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 24:14-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Amenewa adzakweza mau ao, nadzapfuula; cifukwa ca cifumu ca Yehova, iwo adzapfuula zolimba panyanja.

15. Cifukwa cace lemekezani inu Yehova kum'mawa, ngakhale dzina la Yehova, Mulungu wa Israyeli, m'zisumbu za m'nyanja.

16. Kucokera ku malekezero a dziko ife tamva nyimbo zolemekeza wolungama. Koma ine ndinati, Ndaonda ine, ndaonda ine, tsoka kwa ine! amalonda onyenga amangonyenga; inde ogulitsa onyenga apambana kunyenga.

17. Mantha ndi dzenje ndi msampha ziri pa iwe, wokhala m'dziko.

18. Ndipo padzali, kuti iye amene athawa mbiri yoopsya, adzagwa m'dzenje; ndi iye amene aturuka m'kati mwa dzenje, adzakodwa mumsampha, pakuti mazenera a kuthambo atsegudwa, ndi maziko a dziko agwedezeka.

19. Dziko lapansi lasweka ndithu, dziko lapansi lasungunukadi, dziko lapansi liri kugwedezeka kopambana.

20. Dziko lapansi lidzacita dzandi dzandi, ngati munthu woledzera, ndi kunjenjemera, ngati cilindo; ndi kulakwa kwace kudzalilemera, ndipo lidzagwa losaukanso.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 24