Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 24:12-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. M'mudzi mwatsala bwinja, ndi cipata camenyedwa ndi cipasuko.

13. Cifukwa cace padzakhala cotero pakati pa dziko mwa anthu, ngati kugwedeza kwa mtengo waazitona, ngati khunkha la mphesa, pakutha masika ace.

14. Amenewa adzakweza mau ao, nadzapfuula; cifukwa ca cifumu ca Yehova, iwo adzapfuula zolimba panyanja.

15. Cifukwa cace lemekezani inu Yehova kum'mawa, ngakhale dzina la Yehova, Mulungu wa Israyeli, m'zisumbu za m'nyanja.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 24