Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 24:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Taonani, Yehova apululutsa dziko, nalipasula, nalitembenuza dodolido, nabalalitsa okhalamo ace.

2. Ndipo padzakhala monga ndi anthu, moteronso ndi ansembe; monga ndi mtumiki, moteronso ndi mbuyace; monga ndi mdzakazi, moteronso ndi mbuyace wamkazi; monga ndi wogula, moteronso ndi wogulitsa; monga ndi wobwereka, moteronso ndi wombwereka; monga ndi wotenga phindu, moteronso ndi wombwezera phindu kwa iye.

3. Dziko lidzapululuka konse, ndi kupasulidwa ndithu; pakuti Yehova ananena mau amenewa.

4. Dziko lilira nilifota, dziko lilefuka nilifota, anthu omveka a padziko alefuka.

5. Dzikonso laipitsidwa ndi okhalamo ace omwe, cifukwa iwo alakwa pamalamulo nasinthanitsa malemba, natyola cipangano ca nthawi zonse.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 24