Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 23:5-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Pofika mbiriyo ku Aigupto, iwo adzamva kuwawa kwambiri pa mbiri ya Turo.

6. Olokani inu, kunka ku Tarisi, kuwani, inu okhala m'cisumbu.

7. Kodi umene ndi mudzi wanu wokondwa, wacikhalire kale lomwe, umene mapazi ace anaunyamula kunka nao kutari kukhalako?

8. Ndani wapanga uphungu uno pa Turo, mudzi umene upereka akorona, amalonda ace ali akalonga, ogulitsa ace ali olemekezeka pa dziko lapansi?

9. Yehova wa makamu wapanga uphungu uwu, kuipitsa kunyada kwa ulemerero wonse, kupepula onse olemekezeka a m'dziko lapansi.

10. Pita pakati pa dziko lako monga Nile, iwe mwana wamkazi wa Tarisi; palibenso lamba.

11. Iye watambasula dzanja lace panyanja, wagwedeza maufumu; Yehova walamulira za amalonda, kupasula malinga ace.

12. Ndipo Iye anati, Iwe sudzakondwanso konse, iwe namwali wobvutidwa, mwanawamkazi wa Zidoni; uka, oloka kunka ku Kitimu; ngakhale kumeneko iwe sudzapumai.

13. Taonani, dziko la Akasidi; anthu awa sakhalanso; Asuri analiika ilo likhale la iwo okhala m'cipululu; iwo amanga nsanja zao, nagumula nyumba za mafumu ace; nalipasula.

14. Kuwani, inu ngalawa za Tarisi; pakuti linga lanu lapasulidwa.

15. Ndipo padzakhala tsiku limenelo, kuti Turo adzaiwalika zaka makumi asanu ndi awiri, malinga ndi masiku a mfumu imodzi; zitapita zaka makumi asanu ndi ziwirizo, cidzakhala kwa Turo monga m'nyimbo ya mkazi wadama.

16. Tenga mngoli, yendayenda m'mudzi, iwe mkazi wadama, amene unaiwalika; yimba zokoma, curukitsa nyimbo, kuti ukumbukiridwe.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 23