3. Ndipo anthu ambiri adzanka, nati, Tiyeni tikwere kunka ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo; ndipo Iye adzatiphunzitsa za njira zace, ndipo tidzayenda m'mayendedwe ace; cifukwa m'Ziyoni mudzaturuka cilamulo, ndi mau a Yehova kucokera m'Yerusalemu.
4. Iye adzaweruza pakati pa akunja, adzadzudzula mitundu yambiri ya anthu; ndipo iwo adzasula malupanga ao akhale zolimira, ndi nthungo zao zikhale anangwape; mtundu sudzanyamula lupanga kumenyana ndi mtundu wina, ndipo sadzaphunziranso nkhondo.
5. Inu a nyumba ya Yakobo, tiyeni, tiyende m'kuwala kwa Yehova.
6. Cifukwa inu mwasiya anthu anu a nyumba ya Yakobo, cifukwa kuti iwo adzazidwa ndi miyambo ya kum'mawa, ndipo ali olaula ngati Afilisti, naomba m'manja ndi ana a acilendo.
7. Dziko lao ladzala siliva ndi golidi, ngakhale cuma cao ncosawerengeka; dziko lao lidzalanso akavalo, ngakhale magareta ao ngosawerengeka.