Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 14:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pakuti Ambuye adzamcitira cifundo Yakobo, ndipo adzasankhanso Israyeli, ndi kuwakhazikitsa m'dziko la kwao; ndipo acilendo adzadziphatika okha kwa iwo, nadzadzigumikiza ku nyumba ya Yakobo.

2. Ndipo mitundu ya anthu idzawatenga, ndi kuwafikitsa ku malo a kwao; ndipo a nyumba ya Israyeli adzakhala nao amitunduwo m'dziko la Yehova, ndi kuwayesa atumiki ndi adzakazi, ndipo amitunduwo adzatengedwa ndende, ndi amenewo anali ndende zao; ndipo Aisrayeli adzalamulira owabvuta.

3. Ndipo padzakhala tsiku loti Yehova adzakupumitsa cisoni cako, ndi nsautso yako, ndi nchito yako yobvuta, imene anakugwiritsa,

4. pamenepo udzayimbira mfumu ya ku Babulo nyimbo iyi yancinci, ndi kuti, Wobvuta wathadi! mudzi wagolidi wathadi!

Werengani mutu wathunthu Yesaya 14