1. Pakuti Ambuye adzamcitira cifundo Yakobo, ndipo adzasankhanso Israyeli, ndi kuwakhazikitsa m'dziko la kwao; ndipo acilendo adzadziphatika okha kwa iwo, nadzadzigumikiza ku nyumba ya Yakobo.
2. Ndipo mitundu ya anthu idzawatenga, ndi kuwafikitsa ku malo a kwao; ndipo a nyumba ya Israyeli adzakhala nao amitunduwo m'dziko la Yehova, ndi kuwayesa atumiki ndi adzakazi, ndipo amitunduwo adzatengedwa ndende, ndi amenewo anali ndende zao; ndipo Aisrayeli adzalamulira owabvuta.
3. Ndipo padzakhala tsiku loti Yehova adzakupumitsa cisoni cako, ndi nsautso yako, ndi nchito yako yobvuta, imene anakugwiritsa,