Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 13:3-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ine ndalamulira opatulidwa anga, inde, ndaitana amphamvu anga, acite mkwiyo wanga, okondwerera ndi ukuru wanga.

4. Mau a khamu m'mapiri, akunga amtundu waukuru wa anthu, mau a phokoso la maufumu a mitundu yosonkhanidwa! Yehova wa makamu asonkhanitsa khamu kunkhondo.

5. Acokera m'dziko lakutari, ku malekezero a thambo, ngakhale Yehova, ndi zida za mkwiyo wace, kuti aononge dziko lonse.

6. Kuwani inu; pakuti tsiku la Yehova liri pafupi; lidzafika monga cionongeko cocokera kwa Wamphamvuyonse.

7. Cifukwa cace manja onse adzafoka, ndi mitima yonse ya anthu idzasungunuka;

8. ndipo adzaopa; zowawa ndi masauko zidzawagwira; ndipo adzamva zowawa, ngati mkazi wakubala; adzazizwa wina ndi wina; nkhope zao zidzanga malawi a moto.

9. Taonani tsiku la Yehova lidza, lankhanza, ndi mkwiyo ndi kukalipira kwaukali; kupasula dziko, ndi kudzaonongamo akucimwa psiti.

10. Cifukwa nyenyezi za kumwamba ndi makamu ao sizidzawala; dzuwa lidzada m'kuturuka kwace, ndipo mwezi sudzaonetsa kuwala kwace.

11. Ndipo ndidzalanga dziko lapansi, cifukwa ca kuipa kwao, ndi oipa cifukwa ca mphulupulu zao; ndipo ndidzaletsa kudzikuza kwa onyada, ndidzagwetsa kudzikweza kwa oopsya.

12. Ndipo ndidzacepsa anthu koposa golidi, ngakhale anthu koposa golidi weniweni wa ku Ofiri.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 13