Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 13:2-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Kwezani mbendera pa phiri loti se, kwezani mau kwa iwo, kodolani kuti alowe m'zipata za akuru.

3. Ine ndalamulira opatulidwa anga, inde, ndaitana amphamvu anga, acite mkwiyo wanga, okondwerera ndi ukuru wanga.

4. Mau a khamu m'mapiri, akunga amtundu waukuru wa anthu, mau a phokoso la maufumu a mitundu yosonkhanidwa! Yehova wa makamu asonkhanitsa khamu kunkhondo.

5. Acokera m'dziko lakutari, ku malekezero a thambo, ngakhale Yehova, ndi zida za mkwiyo wace, kuti aononge dziko lonse.

6. Kuwani inu; pakuti tsiku la Yehova liri pafupi; lidzafika monga cionongeko cocokera kwa Wamphamvuyonse.

7. Cifukwa cace manja onse adzafoka, ndi mitima yonse ya anthu idzasungunuka;

8. ndipo adzaopa; zowawa ndi masauko zidzawagwira; ndipo adzamva zowawa, ngati mkazi wakubala; adzazizwa wina ndi wina; nkhope zao zidzanga malawi a moto.

9. Taonani tsiku la Yehova lidza, lankhanza, ndi mkwiyo ndi kukalipira kwaukali; kupasula dziko, ndi kudzaonongamo akucimwa psiti.

10. Cifukwa nyenyezi za kumwamba ndi makamu ao sizidzawala; dzuwa lidzada m'kuturuka kwace, ndipo mwezi sudzaonetsa kuwala kwace.

11. Ndipo ndidzalanga dziko lapansi, cifukwa ca kuipa kwao, ndi oipa cifukwa ca mphulupulu zao; ndipo ndidzaletsa kudzikuza kwa onyada, ndidzagwetsa kudzikweza kwa oopsya.

12. Ndipo ndidzacepsa anthu koposa golidi, ngakhale anthu koposa golidi weniweni wa ku Ofiri.

13. Cifukwa cace ndidzanthunthumiritsa miyamba, ndipo dziko lapansi lidzagwedezeka kucokera m'malo ace, m'mkwiyo wa Yehova wa makamu, tsiku la mkwiyo wace waukali.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 13