Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 10:24-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Cifukwa cace atero Ambuye; Yehova wa makamu, Inu anthu anga okhala m'Ziyoni, musaope Asuri; ngakhale amenya inu ndi cibonga, kapena kukusamulira iwe ndodo yace, monga amacitira Aigupto.

25. Pakuti patsala kamphindi, ndipo ukali udzathedwa ndi mkwiyo wanga wakuwaononga.

26. Ndipo Yehova wa makamu adzamuutsira cikoti, monga m'kuphedwa kwa Midyani pa thanthwe la Orebu; ndipo cibonga cace cidzakhala pamwamba pa nyanja, ndipo adzaisamula monga anacitira Aigupto,

27. Ndipo padzakhala tsiku lomwelo, kuti katundu wace adzacoka pa phewa lako, ndi gori lace pakhosi pako; ndipo gori lidzathedwa cifukwa ca kudzoza mafuta.

28. Wafika ku Aiati, wapitirira kunka ku Migroni; pa Mikimasi asunga akatundu ace;

29. wapita pampata; wagona pa Geba, Rama anthunthumira; Gibeya wa Sauli wathawa.

30. Pfuula ndi mau ako iwe mwana wamkazi wa Galimu! tamva, iwe Laisa! iwe Anatoti wosauka!

31. Madimena ali wothawathawa; okhala m'Gebimu asonkhanakutiathawe.

32. Lero lomwe adzaima pa Nobu; agwedezera dzanja lace pa phiri la mwana wamkazi wa Ziyoni, phiri la Yerusalemu.

33. Taonani, Ambuye Yehova wa makamu adzasadza nthambi moopsya; ndipo zazitari msinkhu zidzadulidwa, ndipo zazitari zidzagwetsedwa.

34. Ndipo adzadula nkhalango za m'thengo ndi citsulo, ndipo Lebano adzagwa ndi wamphamvu.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 10