Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 10:19-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo mitengo yotsala ya m'nkhalango yace idzakhala yowerengeka, kuti mwana ailembera.

20. Ndipo padzakhala tsiku lomwelo, kuti otsala a Israyeli, ndi iwo amene anapulumuka a nyumba ya Yakobo, sadzatsamiranso iye amene anawamenya; koma adzatsamira Yehova Woyera wa Israyeli, ntheradi.

21. Otsala adzabwera, otsala a Yakobo, kwa Mulungu wamphamvu.

22. Popeza ngakhale anthu anu Israyeli akunga mcenga wa kunyanja, otsala ao okha okha adzabwera; cionongeko catsimikizidwa, cilungamo cace cisefukira.

23. Pakuti Ambuye Yehova wa makamu adzacita cionongeko cotsimikizidwa pakati pa dziko lonse lapansi.

24. Cifukwa cace atero Ambuye; Yehova wa makamu, Inu anthu anga okhala m'Ziyoni, musaope Asuri; ngakhale amenya inu ndi cibonga, kapena kukusamulira iwe ndodo yace, monga amacitira Aigupto.

25. Pakuti patsala kamphindi, ndipo ukali udzathedwa ndi mkwiyo wanga wakuwaononga.

26. Ndipo Yehova wa makamu adzamuutsira cikoti, monga m'kuphedwa kwa Midyani pa thanthwe la Orebu; ndipo cibonga cace cidzakhala pamwamba pa nyanja, ndipo adzaisamula monga anacitira Aigupto,

27. Ndipo padzakhala tsiku lomwelo, kuti katundu wace adzacoka pa phewa lako, ndi gori lace pakhosi pako; ndipo gori lidzathedwa cifukwa ca kudzoza mafuta.

28. Wafika ku Aiati, wapitirira kunka ku Migroni; pa Mikimasi asunga akatundu ace;

29. wapita pampata; wagona pa Geba, Rama anthunthumira; Gibeya wa Sauli wathawa.

30. Pfuula ndi mau ako iwe mwana wamkazi wa Galimu! tamva, iwe Laisa! iwe Anatoti wosauka!

Werengani mutu wathunthu Yesaya 10