Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 9:6-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ukhala pakati pa manyengo m'manyengo; akana kundidziwa, ati Yehova.

7. Cifukwa cace atero Yehova wa makamu, Taonani, ndidzawasungunula, ndi kuwayesa, pakuti ndidzacitanji, cifukwa ca mwana wamkazi wa anthu anga?

8. Lilime lao ndi mubvi wakuphera; linena manyengo; wina anena mtendere ndi mnansi wace pakamwa pace, koma m'mtima mwace amlalira.

9. Kodi sindidzawalanga cifukwa ca izi? ati Yehova; kodi moyo wanga sudzabwezera cilango mtundu wotere?

10. Cifukwa ca mapiri ndidzagwa misozi ndi kulira, cifukwa ca mabusa a cipululu ndidzacita maliro, cifukwa apserera, kuti anthu sangathe kupitirirapo; ndiponso anthu sangathe kumva mau a ng'ombe zao; mbalame za mlengalenga ndi nyama zathawa, zapita.

11. Ndipo ndidzayesa Yerusalemu miyulu, mbuto ya ankhandwe; ndipo ndidzayesa midzi ya Yuda bwinja, lopanda wokhalamo.

12. Wanzeru ndani, kuti adziwe ici? ndani iye amene kamwa la Yehova lanena naye, kuti acilalikire? cifukwa cace dziko litha ndi kupserera monga cipululu, kuti anthu asapitemo?

13. Ndipo Yehova ati, Cifukwa asiya cilamulo canga ndinaciika pamaso pao, ndipo sanamvera mau anga, osayenda m'menemo;

14. koma anatsata kuuma kwa mtima wao, ndi Baala, monga makolo ao anawaphunzitsa;

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 9