Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 9:17-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Atero Yehova wa makamu, Kumbukirani inu, ndi kuitana akazi akulira, adze; aitaneni akazi ocenjera, kuti adze;

18. afulumire, atikwezere ife mau a maliro, kuti maso athu agwe misozi, ndi zikope zathu ziyendetse madzi.

19. Pakuti mau a kulira amveka m'Ziyoni, Tafunkhidwa, tanyazitsidwa, pakuti tasiya dziko, pakuti agwetsa zokhalamo zathu.

20. Koma imvani mau a Yehova, akazi inu, khutu lanu lilandire mau a pakamwa pace, phunzitsani ana anu akazi kulira, ndi yense aphunzitse mnzace maliridwe ace.

21. Pakuti imfa yakwera m'mazenera athu, yalowa m'nyumba mwathu; kucotsa ana kubwalo, ndi: anyamata kumiseu.

22. Nenani, atero Yehova, Mitembo yathu idzagwa ngati ndowe pamunda, ndi monga cipukutu pambuyo pa wakusenga, palibe wocitola.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 9