Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 8:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Pakuti, taonani, ndidzatumiza pa inu njoka, mphiri, zosalola kuitanidwa; ndipo zidzakulumani inu, ati Yehova.

18. Ha, ndikadatonthoza mtima wanga kuletsa cisoni cace! mtima wanga walefuka m'kati mwa ine.

19. Taonani, mau a kulira kwa mwana wamkazi wa anthu anga ocokera ku dziko lakutari: Kodi m'Ziyoni mulibe Yehova? Kodi mulibe Mfumu yace? Cifukwa canji andiputa Ine ndi mafano ao osema, ndi zacabe zacilendo?

20. Masika apita, mphakasa yatha, ndipo ife sitinapulumutsidwe.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 8