Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 51:37-47 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

37. Ndipo Babulo adzasanduka miunda, mokhala ankhandwe, cizizwitso, cotsonyetsa, wopanda okhalamo.

38. Adzabangula pamodzi ngati misona ya mikango; adzacita nthulu ngati ana a mikango.

39. Pamene atentha, ndidzakonza madyerero ao, ndidzawaledzeretsa, kuti asangalale, agone cigonere, asanyamuke, ati Yehova.

40. Ndidzawagwetsa kuti aphedwe manga nkhosa zamphongo, ndi atonde.

41. Sesake wagwidwatul cimene dziko lonse lapansi linacitamanda calandidwa dzidzidzi Babulo wakhalatu bwinja pakati pa amitundu

42. Nyanja yakwera kufikira ku Babulo; wamira ndi mafunde ace aunyinji.

43. Midzi yace yakhala bwinja, dziko louma, cipululu mosakhalamo anthu, mosapita mwana wa munthu ali yense.

44. Ndipo Ine ndiweruza Beli m'Babulo, ndipo ndidzaturutsa m'kamwa mwace comwe wacimeza; ndipo amitundu sadzasonkhaniranso konse kwa iye; inde, khoma la Babulo lidzagwa.

45. Anthu anga, turukani pakati pace, mudzipulumutse munthu yense ku mkwiyo waukali wa Yehova.

46. Mtima wanu usalefuke, musaope cifukwa ca mbiri imene idzamveka m'dzikomu; pakuti mbiri idzafika caka cina, pambuyo pace caka cina mbiri yina, ndi ciwawa m'dziko, wolamulira kumenyana ndi wolamulira.

47. Cifukwa cace, taonani, masiku alinkudza, amene ndidzaweruza mafano osemasema a Babulo, ndipo dziko lace lonse lidzakhala ndi manyazi; ndipo ophedwa ace onse adzagwa pakati pace.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 51